Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Tikambe zabwino za dziko lathu — JB

Mtsogoleri wakale wa dziko lino, Dr Joyce Banda, wapempha a Malawi kuti adzikamba zinthu zabwino zokhudza dziko lino kuti lipite patsogolo.

Dr Banda, omwe ndi mtsogoleri wa chipani cha PP, amayankhula izi pa msonkhano omwe anachititsa pa bwalo la Nancholi m’boma la Blantyre.

Iwo ati aMalawi ambiri akugwiritsa ntchito masamba a mchezo molakwika ponyoza dziko lino, zomwe ati ndi zomvetsa chisoni.

Mtsogoleriyu watinso mavuto a dziko lino kuti athe akufunika m’gwirizano pakati pa boma, zipani za ndale komanso mabungwe omwe si aboma.

Dr Banda anamemanso a Malawi kuti apitilire kugwira ntchito molimbika ndi cholinga chotukula miyoyo yawo.

Olemba: Blessings Cheleuka
#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Mchinji launches K1.1 billion GESD Projects

Romeo Umali

Malawi advancing clean energy agenda — AG

Secret Segula

GOVT LAUDS MARANATHA ACADEMY

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.