Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Thetsani nkhanza kwa anthu achialubino’

Bungwe la Standing Voice lapempha aMalawi kuti achilimike pothandiza kuthetsa nkhanza zomwe anthu ena amachitira anthu achialubino pomaimba lamya ku ma nambala awulele, kupereka uthenga akaona nkhanzazi.

Ma nambalawo ndi 4293, 116, 5600 ndi 6600.

Atsogoleri a bungweli, limene limalimbikitsa ufulu wa anthu a chialubino, anena izi pa misonkhano yomwe akhala akuchita limodzi ndi bungwe la YONECO m’boma la Mulanje ndi cholinga chophunzitsa anthu za ufulu wa anthuwa.

Mabungwewoo akugwira ntchitoyi limodzi ndi apolosi komanso nthambi ya boma yoona zachisamaliro cha anthu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Achinyamata awapempha kuti athandize boma pa chitukuko

Blessings Kanache

NRB yalemba anthu opitilira 1.5 miliyoni mu ndondomeko yakalembera

Trust Ofesi

Vuto lakuthimathima kwa magetsi Latha kunyumba yamalamulo

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.