Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Olemba nkhani awalangiza kuti afalitse nkhani zokhudza matenda a nkhawa ndi muubongo

Mlembi wamkulu wa bungwe la Malawi Redcross Society, Chifundo Kalulu l, wapempha olemba nkhani kuti agwiritse ntchito ukadaulo wawo polemba nkhani zokhudza matenda a nkhawa komanso amuubongo.

Kalulu amalankhula izi m’boma la Salima pamkumano wa pa chaka wa bungwe la olemba nkhani am’chigawo chapakati la Bwaila Media Club.

Iwo ati atolankhani atha kuthandiza kuphunzitsa anthu za kuwopsya kwa matendawa komanso kufunika kopeza thandizo mwansanga.

“Nkhani ya matenda a nkhawa komanso amuubongo ndi yomwe ikuchititsa kuti chiwerengero cha anthu odzipha chikwere mdziko muno. Kotero ifeyo tikudalira olemba nkhani kuti mutenge uthenga wa mmene anthu angapewere komanso kusaka thandizo pamene akukumana ndi mavuto a muubongo.” Watero Kalulu.

Wapampando wa bungwe la Bwaila Media Club, Felix Washon, wati olemba nkhani m’dziko muno ndi odzipereka kulemba ndi kufalitsa nkhani zomwe zingathandizire kusintha miyoyo ya anthu m’dziko muno.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

OVER 200, 000 JABBED AGAINST COVID -19 IN MANGOCHI

MBC Online

UNICEF remains committed to improve child services in Malawi

Foster Maulidi

CDH Investment Bank donates K2 million for KUHeS research conference

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.