Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

‘Nyumba yamalamulo ya ana ikufunika thumba lapadera’

Komiti ya kunyumba ya malamulo yowona za chisamaliro cha anthu yati dziko lino likufunika thumba lapadera loyendetsera mikumano komanso ntchito za nyumba yamalamulo ya ana achichepere posadalira mabungwe okha.

Wapampando wa komitiyi, a Savel Kafwafwa, ndi amene anayankhula izi Lachisanu masana m’boma la Salima pa msonkhano otseka zokambirana za aphungu akunyumba ya malamulo ya ana achichepele m’bomalo.

A Kafwafwa anati izi ziyenera kudzera kunyumba yamalamulo komanso ma khonsolo a m’mizinda chifukwa kutero zithandizira kuti ntchito zamtunduwu zizipitililabe ngakhale kuti mabungwe ena atamaliza ntchito zawo.

Mlembi ku unduna oona za chisamaliro cha anthu, a Nwazi Mnthambala, anati ndi zofunikadi kuti zokambirana za ana zamtunduwu zikhazikike mu ndondomeko za boma zomwe zilipo kuti ntchitoyi ikhazikike m’dziko muno.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Paramount Gomani V calls on Maseko Ngoni to live peacefully with other tribes

MBC Online

Awiri aphedwa polimbilana ufumu wa Mankhamba

Austin Kachipeya

Govt commends partnership in promotion of inclusive development

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.