Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati akufunitsitsa kuti anthu adzigula katundu otsika ndipo wati izi ndi zotheka kudzera mu chitukuko cha njanji.
Iye wati chitukuko cha njanji chalimbikitsanso ubale ndi mgwirizano ndi mayiko ozungulira monga Mozambique ndi Zambia.
Dr Chakwera atinso akufunitsitsa kuti anthu adzikhala ndi chuma kudzera mundondomeko za boma, kuphatikizapo ngongole za NEEF, ndipo ati ndi masomphenya a chipani cha Malawi Congress (MCP) kuti idzale Njanji.
Iwo anapitilira kunena kuti zovuta zomwe zilipo boma likukonza ndipo zinthu zakhala bwino.
“Zitukuko zikupitilira ndipo ndizolimba,” anayankhula motero President Chakwera.
Dr. Chakwera wapemphanso anthu a m’boma la Nsanje kuti adzamuvotere komanso aphungu achipani cha MCP.
Pa msonkhanowu panalinso wachiwiri kwa mtsogoleri wa MCP m’chigawo cha kummwera, a Abida Mia, ndi akuluakulu ena a chipani MCP.
Olemba: Mercy Zamawa

