Malawi Broadcasting Corporation
Business

National Bank yapanga phindu lokwana K42.1 billion mu miyezi isanu ndi umodzi

Banki ya National yapanga phindu lokwana K42.1 billion mu miyezi yapakati pa January mpaka June chaka chino.

Izi ndi malinga ndi kalata yazachuma yomwe bankiyi yatulutsa ndipo yasayinidwa ndi mkulu wa bankiyi a Harold Jiya komanso wapampando wake a Jimmy Lipunga mwa ena.

Phinduli ndilokwera ndi ma peresenti 19 poyerekeza ndi K35.5 billion yomwe bankiyi inapeza nthawi ngati yomweyi chaka chatha.

Kalatayi yati phinduli lapezeka kaamba koti ndalama zomwe makasitomala anasungitsa zinachuluka zomwe zapangitsa kuti anthu akongole zambiri.

Banki ya National ndi imodzi mwa banki zomwe ziri pa msika wamasheya wa Malawi Stock Exchange.

Related posts

Consider Art as a Business — Chomanika

Romeo Umali

CHAKWERA MEETS SMALL-SCALE BUSINESS PLAYERS

McDonald Chiwayula

EDF in a drive to restore degraded environments

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.