Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

Mzuzu Technical College ili ndi ngongole ya K65 million

Sukulu ya luso lamanja ya Mzuzu ili pachiopsyezo chosatsegulira mwezi wa mawawu kaamba ka ngongole yoposa K65 million imene ili nayo.

Mkulu wa sukuluyi, a Julius Phiri, wanena izi pomwe nthambi yakunyumba yamalamulo imene imalondola ndalama zaboma ya Public Accounts Committee (PAC) imakumana mu mzinda wa Mzuzu.

“Pamwezi timayenera tilandire ndalama yoposa K10.5 million. Takhala tikutenga ngongole komanso kulephera kubweza ngongole ku makampani amene amatigulitsa zinthu zoyendetsera sukulu kuphatikizapo chakudya,” iwo anatero.

Wapampando wa PAC, a Mark Botoman, anati ndi okhumudwa chifukwa sukulu yokhayo imene ikusula luso la ntchito zamanja ku Mzuzu ikukumana ndi mavuto azachuma mpaka kufuna kuyitseka.

“Ife ngati komiti yakunyumba yamalamulo tiyankhulana ndi akuluakulu aku unduna wazachuma kuti ndalama zifike mwansanga pa sukulu pano,” a Botoman anatero.

Boma limathandiza sukulu ya Mzuzu Technical College. M’mbuyomu, a mpingo wa Katolika nawonso ankhathandizira koma anasiya.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Masewero opalasa njinga ali ndi tsogolo’

MBC Online

ALL SET FOR OFFICIAL OPENING OF KALIPANO HOTEL BY SUNBIRD

McDonald Chiwayula

Christ Alive Family Church marks 20 years of service

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.