Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Mwaungulu tsopano adzivala Jersey 11

Osewera kutsogolo wa timu ya FCB Nyasa Big Bullets, Patrick Mwaungulu, amupatsa nambala 11 yomwe adzivala pa Malaya ake a timuyi.

Izi zadziwika mu chikalata chimene atulutsa a timu ya Bullets pamene amatulutsa m’ndandanda wa osewera a timuyi mu chaka cha 2024.

Mwaungulu amusintha kuchoka pa nambala 29 yomwe amupatsa Chawanangwa Gumbo, amene poyamba amavala nambala 31.

Osewera ena monga Clyde Senaji, Richard Chimbamba, Yankho Singo, Kenneth Pasuwa ndi Ephraim Kondowe nawonso awasinthira nambala zawo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi finishes 7th at AFCON Beach Soccer

Romeo Umali

Salima Sugar ikupereka K500 million kwa osamuka m’minda yawo

Foster Maulidi

Security agencies urged to promote gender inclusion

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.