Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Mtsogoleri wa FIFA akapepesa maliro a Dr Chilima

Mtsogoleri wa bungwe loyang’anira masewero a mpira wa miyendo padziko lonse la pansi la FIFA, a Gianni Infantino, akuyembekezeka kupepesa mwapadera ku banja la malemu Dr Saulos Chilima amene anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino.

Iwo akapepesanso kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

A Infantino afika m’dziko muno lachiwiri madzulo kudzera pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe pamene analandiridwa ndi mtsogoleri oyendetsa masewero a mpira wa miyendo m’dziko muno, a Fleetwood Haiya.

Koma a Infantino ayimitsa kaye dongosolo limene anakonza kuti ayambepo ntchito yoyendera masewero a mpira wa miyendo kaamba ka chisoni chomwe chakuta dziko la Malawi.

 

 

Related posts

Ku Mingoli Bash sikukhala oyimba akunja

Romeo Umali

Tourism Minister presides over Holi festival celebration

Rabson Kondowe

KK, Likoma triumph in 2024 swimming contest

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.