Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Magetsi ndi awa koma asamaleni- Matola

Nduna yowona za mphavu yamagetsi, a Ibrahim Matola, lero ayendera ntchito yolumikiza magetsi kumadera akumudzi yotchedwa Malawi Rural Electrification Program – MAREP phase 9 kumadera a Choma ku Mzimba ndi Ruviri komaso Chozoli m’boma la Rumphi.

Ntchitoyi yomwe yafika gawo lolumikiza ma transformer ithandizira zipatala, sukulu, mabizinesi ndi nyumba za anthu omwe akukhala madera  akumudzi komwe sikunafike  magetsi.

A Matola alimbikitsa mafumu ndi anthu awo kuti asamalire chitukukochi kaamba koti boma lalowetsa ndalama zambiri powonetsetsa kuti midzi yonse ikhale ndi magetsi mdzikomuno

Group Village Elton Zika Chimaliro omwe akuyimilira midzi yokwana zisansu ndi ziwiri -12 yomwe itapindule ndi ntchitoyi , ati tsopano ndiwokondwa popeza poyamba analibe chiyembekezo kuti magetsiwa atha kufika ku dera kwawo.

Iwo ati akuyembekezera kuti izi zithandizira kuti ana a sukulu  azichita bwino pa maphunziro awo.

 

Olemba Yamikani Makanga

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Flue Cured tobacco hits over four dollars

MBC Online

Unduna wa za ulimu watulutsa mitengo ya mbewu

Justin Mkweu

Norwegian govt committed to ensuring Malawians register for votes

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.