Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local Local News Nkhani

Komiti ya COVID 19 siyinayankhulebe pa malipoti akubuka kwa nthendayi

Komiti yoona za matenda a Covid 19 siyidayankhulepo kanthu pambuyo pa malipoti osonyeza kuti munthu m’modzi wapezeka ndi nthendayi m’boma la Mangochi.

Malinga ndi mmodzi mwa madotolo apachipatala chachikulu cha Mangochi, Innocent Lanjesi, mayi wazaka 32 mdera lamfumu yaikulu Makanjira ku Mangochi wapezeka ndimatenda a COVID 19.

Iwo ati izi zadziwika pamene madotolo osiyanasiyana ali mderali kuthandiza anthu ochokera mmadera akutali oti sangakwanitse kukafika kuchipatala chachikulu cha Mangochi.

Madotolowa ali ku Makanjira ndibungwe lachifundo laku German la Hilal Africa.

MBC Digital inayesayesa kufuna kumva kuchokera kwa akuluakulu a COVID-19 Committee komanso ku unduna wa zaumoyo amene panthawiyo samapezeka.

Dr. Lanjesi ati panopa mayiyu amutumiza kuchipatala chachikulu cha Mangochi kukalandira thandizo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Patriots donate medical equipment to Likuni Mission Hospital

MBC Online

Tisagwire ntchito monyinyilika -Chakwera

McDonald Chiwayula

UN Women launches strategic note to drive gender equality in Malawi

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.