Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bangwe yapha Bullets

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yagonja ndi timu ya Bangwe All Stars 1-0 pa bwalo la masewero la Kamuzu kudzera mu chigoli cha James Msowoya.

Aka ndi kugonja kachitatu kwa Bullets mu 2024 TNM Super League imene ili pa nambala khumi pa mdandanda wa matimu amu ligiyi.

Kupambanaku, zikutanthauza kuti Bangwe tsopano ili ma nambala 15 pa mdandanda wa matimuwa ndi ma point okwananso 15.

Awatu ndi masewero oyamba kuti timuyi igonjetse amene akusungira chikhochi komanso koyamba kuti achinye pagolo pawo pamasewero asanu amene asewera limodzi.

Komanso, awa anali masewero achiwiri a Trevor Kajawa chilhalireni ngati mphunzitsi wa tsopano wa Bangwe.

 

Olemba: Praise Majawa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

SAUDI GOVT COMMITS $25 BN INVESTMENTS IN AFRICA

MBC Online

BANK DONATES TOWARDS MALAWI LAW SOCIETY AGM

Charles Pensulo

Chimwendo praises MCP unity ahead of 2025 elections

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.