Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

CRWB ipereka mphoto kwa makasitomala okhulupirika

Bungwe la Central Region Water Board (CRWB) lapereka mphoto kwa ena mwa makasitomala ake omwe amalipira madzi mokhulupirika.

Cholinga cha mphotozi ndi kufuna kulimbikitsa anthu ena, zimene akuti zikhoza kuthandiza kukweza ndi kupititsa patsogolo ntchito yogawa madzi chigawo chonse chapakati.

Ofalitsankhani ku CRWB, a Zephelino Mitumba, ndi amene ananena izi pa mwambowo umene umachitikira pa bwalo la masewero la Dowa Community m’boma la Dowa.

Iwo anati pali mavuto ambiri amene amakumananawo pa ntchito yopereka madzi, zimene zimachititsa kuti masiku ena madzi asamatuluke m’mipopi.

Makasitomala makumi atatu ndi amene alandira mphoto pa mwambowo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

GOVT TOUTS ISRAEL LABOUR EXPORT DEAL AS FOREX SPINNER

Eunice Ndhlovu

Awamanga ataba mabisiketi ku kampani ya Universal

Charles Pensulo

Mother of seven receives aid from Lions Club following appeal

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.