Malawi Broadcasting Corporation
International News

Apolisi amanga munthu amene amafuna kupha Trump

Apolisi m’dziko la America amanga a Vem Miller, 49, powaganizira kuti amafuna kupha mtsogoleri wakale wa dzikolo, a Donald Trump.

Malinga ndi ofalitsankhani wa apolisi kumeneko, a Chad Bianco, oganiziridwayu, yemwe amanamizira kuti ndi mtolankhani, anamugwira akufuna kulowa pa zipata za bwalo la Coachella Valley ku California komwe a Trump amachititsa msonkhano okopa anthu.

Apolisi atafufuza m’galimoto mwa a Miller anapezamo mfuti ziwiri, zipolopolo zochuluka komanso ziphaso zoyendera zachinyengo zomwe zinali ndi mayina a anthu osiyanasiyana.

A Miller akhala munthu wachitatu kumangidwa poganiziridwa kuti amafuna kupha a Trump.

A Trump, omwe ndi achipani chotsutsa cha Republican, ndi mmodzi mwa anthu omwe akupikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa dzikolo pa zisankho zomwe zichitike mu November chaka chino.

Olemba: Alufisha Fischer

Related posts

Climate Smart Programme participants receive wages

Romeo Umali

Human rights expert urges renewed approach to uphold right to food

Romeo Umali

Japan celebrates 60 years of development in Malawi

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.