Apolisi m’boma la Mangochi amanga a Arnold Moyowatha, 54, powaganizira kuti anabaya pamimba wapolisi pamene amafuna kuti awamange.
Ofalitsa nkhani za apolisi m’bomali, a Amina Tepani Daudi, ati izi zinachitika pamene apolisi anali pa ntchito yawo yoyendera m’madera amene kumachitika umbanda ndipo a Moyowatha anali ndi anzawo ena awiri amene anathawa.
A Daudi ati pamene a Moyowatha amafuna kuti adzipulumutse anatulutsa mpeni ndi kuvulaza wapolisiyo amene anathamangira naye kuchipatala ndipo anakalandira thandizo.
A Moyowatha ali m’chitokosi pamene akudikira kukaonekera kubwalo la milandu.