Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Malo nawa koma tionepo chitukuko pasanathe zaka ziwiri’

Mwambo opereka malo kwa atsikana osewera mpira wa miyendo mutimu ya Scorchers wayamba ndi kupereka zikalata zaumwini kwa osewerawa ku unduna wa zamalo ku Lilongwe, komwe atsikanawa asonkhana limodzi ndi aphunzitsi awo.

Malinga ndi chikalata chomwe unduna wazamalo wawerenga pamwambowu, atsikanawa akuyembekezeka kupanga chitukuko pamalowa pasanadutse zaka ziwiri ndikuti akalephera kutero, boma lidzatenganso malowa.

Pamwambowu pali akuluakulu a ku unduna wa za malo, unduna wa zamasewero komanso akuluakulu a bungwe loyendetsa mpira wa miyendo m’dziko muno la Football Association of Malawi ndipo mlendo olemekezeka ndi Chikumbutso Mtumodzi, mlembi wamkulu oyang’anira ntchito zosiyanasiyana ku unduna wa zamasewero.

Related posts

‘Ubale wa dziko la China ulimbikitse Malawi pa ntchito zamalonda’

Rabson Kondowe

Mabedi wavomereza kuti Flames ili mu gulu lovuta mu AFCON 2025

MBC Online

Chilima, nine others killed in plane crash

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.