Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Malizani msewu mu nthawi yake — PAC

Wapampando wa komiti ya Public Accounts a Mark Botomani ati ndi okhumudwa kaamba ka kuchedwa komaliza kwa ntchito yokonza msewu wa pa Kammwamba.

Msewuwu ndi otalika makilomita asanu ndi imodzi ndipo uli mbali imodzi yakonzanso msewu wa Zalewa kupita kwa Chingeni m’boma la Balaka, omwe ndi otalika makilomita pafupifupi 65.

Izi zikutsatira zokambirana zomwe a Road Fund Administration anachita ndi komitiyi zokhudza msewuwu.

Kontalakitala yemwe akukonza msewuwu wati mwa zina, kutsika mphamvu kwa ndalama ya klKwacha ndi kumene kwachedwetsa ntchitoyi.

Poyankhula atawuyendera, a Botomani anati afikanso pa malopa pakadutsa miyezi itatu pamene akaone m’mene ntchitoyi ikuyendera pomwe nthawi yake yomwe anakonza kuti ukhale utatha yadutsa.

Wapampando wa bungwe la National Roads Fund Administration, a Matthews Chikakheni, anatsimikiza kuti ndalama zogwilira ntchitoyi zilipo ndipo a Malawi asade nkhawa poti ntchitoyi yayambilanso ndipo makontalakitala atsimikiza kuti itha nyengo ya mvula isanafike.

Ntchitoyi inayamba m’mwezi wa July cha chatha ndipo imayembekezeka kutha mwezi uno.

Olemba: Naomi Kamuyango

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Wapereka mimba kwa mwana wobereka yekha

Charles Pensulo

ESCOM builds 29 modern houses for Neno and Mwanza communities

MBC Online

2024 SONA IN SYNC WITH MW 2063 — NPC

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.