Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

‘Dziko la Mozambique ndi lofunika pa chitukoko chathu’

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, wati aMalawi akuyenera kugwira ntchito molimbikira kuti dziko lino lipeze chuma.

Dr Chakwera ati zina mwa ntchito zimene zikugwiridwa m’dziko lino zikutheka kaamba kaubale wabwino umene ulipo pakati pa dziko la Malawi ndi la Mozambique, kudzera mwa mtsogoleri wa dzikolo, Dr Filipe Jacinto Nyusi.

Dr Chakwera atinso kudzera mu ulimi, dziko lino litukuka maka likatsatira njira zamakono zaulimi.

Iye amayankhula potsekulira chionetsero cha malonda a zaulimi, pamodzi ndi Dr Nyusi, mu mzinda wa Blantyre.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NEEF yati ipitilira kuthandiza anthu

MBC Online

Fuel Shortage to end soon — NOCMA

Beatrice Mwape

Chakwera arrives in Karonga

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.