Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Nkhani Politics

Anthu aku Ntcheu ayamika boma chifukwa cha ngongole ya K2.1 billion kwa alimi

Senior Chief Mpando yakwa Kambilonjo ku Ntcheu, yayamika boma chifukwa chopereka ngongole yokwana K2.1 billion kwa anthu m’bomali kudzera ku NEEF.

Pomulandira President Chakwera, Senior Chief Mpando yati ngongole zimenezi zalimbikitsa ulimi kaamba koti anthu akulima katatu pachaka tsopano.

Mfumuyi yati anthu akugula mbewu komanso ma pump ochitira ulimi wanthilira.

Komabe mfumuyi yapempha boma kuti limalize kupaka phula msewu wa pakati pa Tsangano ndi Neno omwe wadutsa mderalo.

Iwo apemphanso boma kuti likonze ndondomeko yothandiza kuti anthu adzipindula ku ntchito za mgodi omwe uli mderalo.

Yemwe ayimire chipani cha MCP ngati phungu wadera la Dzonzi Mvai, a Mwayi Kamuyambeni, apempha madzi abwino, chakudya komanso mlatho pa mtsinje wa Thava omwe umalumikiza anthu a mdera la Kambilonjo ndi Phalula m’boma la Balaka.

Olemba: Isaac Jali

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

World Sharp graduates over 600 students

Paul Mlowoka

Kalindo has a case to answer

Blessings Kanache

Madzi aukhondo afika ku Mphampha ndi Tsambalabooka m’boma la Chikwawa

Charles Pensulo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.