Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Timalizitsa msewu wapakati pa Tsangano ndi Neno — Chakwera

President wa dziko lino yemwenso ayimire chipani cha Malawi Congress, Dr Lazarus Chakwera, watsimikizira anthu m’boma la Ntcheu kuti boma limaliza kupaka phula msewu wa pakati pa Tsangano ndi Neno.

President Chakwera wanena zimenezi pa sitolo zapa Kambilonjo, kuzambwe kwa boma la Ntcheu.

Dr Chakwera wati ndalama za msewuwo zilipo kale ndipo akudziwa kuti msewu wamakono udzathandiza pa ntchito za malonda ndi ulimi.

Iwo anati ndi okondwa kuti anthu m’boma la Ntcheu apindula ndi ngongole ya NEEF, komwe NEEF yapereka K2.1 billion.

Dr Chakwera watsimikizira anthu omwe sanapeze mwayi wa ngongolezo kuti NEEF ipitiriza kupereka ngongole.

Pa nkhani ya migodi, Dr Chakwera anati dziko lino linadalitsika ndi miyala ya mtengo wapatali ndipo ayetsetsa kuti chuma chochoka kumigodi chipindulire aMalawi kudzera ku thumba la Sovereign Fund.

President Chakwera pamenepa anapempha anthuwo kuti adzamuvotere pa chisankho chikudzachi.

Dr Chakwera tsopano akupita kwa Champiti mdera lakumvuma m’boma la Ntcheu.

Olemba: Isaac Jali

Related posts

CS-EPW participants tipped on small scale businesses

Romeo Umali

Ministry of Health achieves 61% cervical cancer treatment rate

McDonald Chiwayula

MEC holds public lecture in Zomba

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.