Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Shuga wafika wambiri pa msika – Kunkuyu

Nduna yazofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu yati boma laonetsa chidwi chachikulu kuti shuga apezeke paliponse m’dziko muno.

Poyankhula ndi MBC ku Lilongwe a Kunkuyu ati kampani ya Salima Sugar yomwe panopa ili m’manja mwa boma la Malawi yayamba tsopano kufikitsa shuga msitolo zosiyanasiyana.

Izi zikudza pomwe kampani ya Salima Sugar kudzera mwa Takula Group of Companies, mmawa wa lero lachisanu yatsitsa shuga wokwana matani makumi atatu mu mzinda wa Lilongwe m’ma shop a Tutla’s.

M’modzi mwa akuluakulu a Kampani ya Takula, a Takondwa Kathumba ati akukonzanso dongosolo loti akasiye shuga okwana matani 85 ku Shoprite komanso matani 20 ku sitolo ya Ekhaya.

A Kunkuyu ati anthu ambili andale m’mbuyomu analowelera ntchito  za kampani ya Salima Sugar zomwe zinachititsa kuti ntchito yopanga shuga kukampaniyi ilowe pansi.

Iwo ati boma likuchita chilichonse chotheka poonetsetsa kuti shuga azipezeka mdziko muno komanso pa mtengo wabwino.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Treasury takes ATM Strategy to China forum

Justin Mkweu

MBS donates wheelchairs to Kachere Rehab

Chisomo Break

MAGU She-Wolves defend Mo626 title

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.