Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

President Chakwera acheza ndi anthu ku Lilongwe

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, acheza ndi anthu m’madera angapo m’boma la Lilongwe, lero Lachitatu.

Dr Chakwera ayambira kucheza ndi anthu a kwa Chiuzira kenako kwa Pondamali, akachoka apo apita kwa Chiseka, kenako ku Mitundu, kwa Maluwa ndipo amaliza ndi kwa Kacheta.

Padakalipano, khwimbi la anthu lasonkhana kale pa Chiuzira kudikira kufika kwa President Chakwera.

Kudzera ku misonkhano imeneyi, mtsogoleri wa dziko linoyu afotokozera anthu ntchito za chitukuko zimene boma likugwira, komanso zimene likuchita powathandiza pa mavuto monga njala, komanso kumva mavuto ena amene anthu akukomana nawo.

Sabata zingapo zapitazi, Dr Chakwera anayendera anthu ku Nkhotakota, Dedza, Dowa, Mchinji ndi Kasungu.

Olemba: Isaac Jali

Related posts

Elderly woman dies after wall collapses on her

Romeo Umali

Malawi to celebrate its first World Creativity and Innovations Day

Romeo Umali

Malawi U-21 Korfball Team Beats Zimbabwe 7-3

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.