Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

M’nyamata wa zaka 17 adziombera chifukwa cha chikondi

M’nyamata wazaka 17 zakubadwa, Tinasha Mtawali, wafa atadziombera ndi mfuti ya mtundu wa pistol ku Chitipi munzinda wa Lilongwe chifukwa anasemphana chichewa ndi bwenzi lake, malinga ndi ofalitsankhani ku Polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu.

Iwo ati Mtawali anachoka kwawo ndikupita malo ena osadziwika kumene anayimbira lamya bwenzi lakelo ndi kumuuza kuti sadzamuonanso ndipo ali mkati mokambirana, adamva phokoso la kuwomba kwa mfuti kenako sanamvekenso.

Zitatero, a Chigalu ati bwenzi la malemuwa linakanena za nkhaniyi kwa abale ake ndipo bambo ake atayang’ana pamene amasungapo mfuti yawo sanayipeze, zomwe zinachititsa kuti ayambe kumufufuza mpaka atampeza pamalo ena atafa, pambali pake pali mfuti ndi lamya yake.

Achipatala atapima thupi la malemuwa apeza kuti Tinasha anafa chifukwa cha mabala a m’mutu chifukwa cha chipolopolo.

Mtawali adali wa m’mudzi wa Senzani m’boma la Ntcheu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Phyzix set to invade Mzuzu

Kumbukani Phiri

Dedza stands united as they mourn former VP

Sothini Ndazi

MEC ENGAGES ARTISTS IN ELECTORAL PROCESSES AND REFORMS

Salomy Kandidziwa
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.