Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

MBC yachita mgwirizano ndi Water Aid

Nyumba youlutsa mawu ya boma, Malawi Broadcasting Corporation (MBC), yasayina mgwirizano ndi bungwe la Water Aid.

Cholinga cha mgwirizanowu ndi kupititsa patsogolo nkhani zokhudza ukhondo komanso kasamalidwe kamadzi.

Mkulu wa MBC, a George Kasakula, wati wayilesiyi ndiyodzipereka pofalitsa nkhani zachitukuko monga zamtunduwu ndipo alonjeza zokonza ma programme apamwamba okhudza madzi ndi ukhondo.

“Apa zili ngati kukankhira pumbwa kuchipwete chifukwa izi ndi zimene timapanga,” a Kasakula anatero.

Mkulu wa Water Aid m’dziko muno, a Peter Phiri, anayamikira mgwirizanowu ndipo anati akukhulupilira kuti uthandiza kukopa mabungwe ena othandiza pankhani zachuma , makamaka popititsa patsogolo nkhani zachitukuko chamadzi ndi ukhondo m’dziko muno.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Dark and Lovely in-pack shampoo recalled

Earlene Chimoyo

Masewero a Darts m’chigawo chapakati apeza thandizo

Foster Maulidi

Govt to roll out e-payment for SCTP beneficiaries in Mzimba

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.