Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

MBC yachita mgwirizano ndi Water Aid

Nyumba youlutsa mawu ya boma, Malawi Broadcasting Corporation (MBC), yasayina mgwirizano ndi bungwe la Water Aid.

Cholinga cha mgwirizanowu ndi kupititsa patsogolo nkhani zokhudza ukhondo komanso kasamalidwe kamadzi.

Mkulu wa MBC, a George Kasakula, wati wayilesiyi ndiyodzipereka pofalitsa nkhani zachitukuko monga zamtunduwu ndipo alonjeza zokonza ma programme apamwamba okhudza madzi ndi ukhondo.

“Apa zili ngati kukankhira pumbwa kuchipwete chifukwa izi ndi zimene timapanga,” a Kasakula anatero.

Mkulu wa Water Aid m’dziko muno, a Peter Phiri, anayamikira mgwirizanowu ndipo anati akukhulupilira kuti uthandiza kukopa mabungwe ena othandiza pankhani zachuma , makamaka popititsa patsogolo nkhani zachitukuko chamadzi ndi ukhondo m’dziko muno.

Related posts

Khonsolo ikufuna ndalama za chitukuko zidzibwera motsata ndondomeko

Rabson Kondowe

ENERGY MINISTER CALLS FOR MORE FINANCING IN CLEAN COOKING ENERGY

Mayeso Chikhadzula

60,000 illegal fishing gear destroyed in Nkhata Bay

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.