Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Engineer Mumba, Zikhale athandiza Chakwera

Awiri mwa anthu omwe alephera pa chisankho cha wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha Malawi Congress (MCP) Engineer Vitumbiko Mumba komanso a Ken Zikhale Ng’oma ati iwo sagwa mphwayi koma kuthandiza chipanichi kuti chidzapambane pa chisankho cha chaka cha mawa.

Engineer Mumba wati agwira ntchito ndi Dr Chakwera komanso omwe apapambana, Mai Catherine Gotani Hara, polimbikitsa chipani cha MCP komanso kutukula dziko lino.

Nawo a Zikhale polankhakhula atagwirana paphewa ndi a Mumba komanso a Gotani Hara, anati iwo anabweranso kunsonkhanowu ngakhale alephera pofuna kuonetsa kuti sananyanyale koma akukondwera kuti wapambana ndi mzimayi, ndipo agwira limodzi ntchito.

Nawo a Gotani Hara auza MBC kuti akuthokoza Chauta komanso amuna awo powathangata kupambana, ndipo ati azifunsa nzeru ndi upangiri kuchokera kwa anthu omwe agonjawa kaamba ali ndi kuthekera kwina komwe iwo alibe.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Real Estate described as game changer

Charles Pensulo

Titukule sukulu za mkombaphala – Joe Ching’ani

MBC Online

Bucket fund to help young aspirants

Naomi Kamuyango
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.