Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kulimbikitsa ngodya zisanu zamaphunziro

Unduna wamaphunziro wati ukuika chidwi kwambiri pa ngodya zake zisanu zokweza maphunziro kuti maphunziro akhale opindulira ophunzira.

Mlembi wankulu mu Unduna wazamaphunziro a Mangani Katundu wauza MBC kuti mwazina, ngodya zisanuzi zikulunjika pa nkhani yowonetsetsa kuti aphunzitsi akupeza zosowa zawo komanso akuchita maphunziro oyenera asanawalembe ntchito, Kusinthanso ndondomeko ya maphunziro kapena kuti curriculum, kuonesetsa kuti ntchito yogawa phala ifikile sukulu zonse mdzikomuno komanso kulimbikitsa luso lamakono pakati pa ophunzira.

Powonjezera apa, a Katundu ati Unduna wazamaphunziro ukuyesetsanso kuti ophunzira 700,000 omwe analibe mwai ophunzira mzipinda zolongosoka akhale ndi mwayi umenewo kudzera ku ndondomeko Malawi Education Reform Programme (MERP) yomwe yaika padera ndalama zokwana K150 billion zomangira zipinda zamakono zophunziliramo.

 

By Tasungana Kazembe

Related posts

World Vision vows to keep girls in school

MBC Online

MRA to use drones and tax stamps in fight against goods smuggling

McDonald Chiwayula

ESCOM’s OFC injects K10 million into MACRA ICT Awards

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.