Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Ntchito yonyamula zovuta ku Chikangawa yayambika

Apolisi limodzi ndi azachipatala ayamba kunyamula matupi a anthu amene ataya miyoyo yawo pangozi ya ndege imene yagwa chapa Lunjika mu nkhalango ya Chikangawa m’boma la Mzimba.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Saulos Chilima pamodzi ndi akuluakulu ena asanu ndi anayi, apezeka atamwalira pa ngoziyi, malinga ndi kutsimikiza kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera pamene amayankhula kwa mtundu wa Malawi.

Pakali pano, matupi a anthuwo akuyembekezeka kutengedwa kuchoka ku nkhalangoyi kupita ku Capital Hill munzinda wa Lilongwe.

Akuluakulu aboma, aphungu aku nyumba ya malamulo komanso makhansala ndi anthu osiyanasiyana ali pamalowa, pamene asilikali a dziko lino akuyesetsa kukhazikitsa bata ndikutsogolera anthu mwadongosolo pa malowa.

Olemba: Jackson Sichali

Related posts

Chakwera to officially open Zomba Stadium

Romeo Umali

PMRA, WHO to survey substandard, falsified medicines

Romeo Umali

Oganiziridwa za “Bakili Muluzi TV” akudikira kumva za belo

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.