Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Timalizitsa msewu wapakati pa Tsangano ndi Neno — Chakwera

President wa dziko lino yemwenso ayimire chipani cha Malawi Congress, Dr Lazarus Chakwera, watsimikizira anthu m’boma la Ntcheu kuti boma limaliza kupaka phula msewu wa pakati pa Tsangano ndi Neno.

President Chakwera wanena zimenezi pa sitolo zapa Kambilonjo, kuzambwe kwa boma la Ntcheu.

Dr Chakwera wati ndalama za msewuwo zilipo kale ndipo akudziwa kuti msewu wamakono udzathandiza pa ntchito za malonda ndi ulimi.

Iwo anati ndi okondwa kuti anthu m’boma la Ntcheu apindula ndi ngongole ya NEEF, komwe NEEF yapereka K2.1 billion.

Dr Chakwera watsimikizira anthu omwe sanapeze mwayi wa ngongolezo kuti NEEF ipitiriza kupereka ngongole.

Pa nkhani ya migodi, Dr Chakwera anati dziko lino linadalitsika ndi miyala ya mtengo wapatali ndipo ayetsetsa kuti chuma chochoka kumigodi chipindulire aMalawi kudzera ku thumba la Sovereign Fund.

President Chakwera pamenepa anapempha anthuwo kuti adzamuvotere pa chisankho chikudzachi.

Dr Chakwera tsopano akupita kwa Champiti mdera lakumvuma m’boma la Ntcheu.

Olemba: Isaac Jali

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Silver Strikers conclude 2024 TNM Super League in style

Romeo Umali

UTM condemns violence, calls for peace ahead of VP’s burial tomorrow

MBC Online

‘Malo nawa koma tionepo chitukuko pasanathe zaka ziwiri’

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.