Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local Music News

Ku Mingoli Bash sikukhala oyimba akunja

Amene akonza phwando la mayimbidwe la Ku Mingoli Bash achotsa oyimba onse akunja monga Cassper Nyovest ndi Young Stunna pam’ndandanda wa oimba akuphwando la chaka chino.

A Shadreck Kalukusha, amene akuyendetsa phwandoli, ati pakadali pano chidwi chili kwa oyimba aku Malawi amene ati akufuna kuti adziwalemekeza powalipira bwino ndi kuwapatsa zoyenera.

“Tikufuna tipange zosiyana chaka chino, khama limene timayika pa oyimba monga Busy Signal akabwera tiliyike pa Tay Grin kapena Namadingo,” anatero a Kalukusha.

Phwando la Ku Mingoli Bash ndi lachiwiri kuchitika chaka chino pomwe oyimba 27 a m’dziko muno adzayimbe patsikuli m’mwezi wa August pa bwalo la Civo munzinda wa Lilongwe.

 

Related posts

Maranatha Academy rewards MSCE top achievers

McDonald Chiwayula

Drop in maize prices excites LL consumers

Rabson Kondowe

Asthma awareness campaigns are vital — MSAM

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.