Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Tidziganizira momwe tingatukulire maanja athu — Kunkuyu

Nduna yofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu yatsindika zakufunika koti aMalawi adziganiza mozama m’mene angamatukulire maanja awo, madera komanso dziko lonse ngati muja achitira akatswiri osewera mpira wa miyendo.

A Kunkuyu amayankhula izi ku Blantyre pamene amakhazikitsa chikho cha Tambala Super Cup ndipo anati nthawi yakwana yoti anthu adzikhala olimbikira kwambiri pa ntchito zonse zimene zingathandizire kupititsa patsogolo miyoyo yawo.

Iwo anadzudzulanso m’chitidwe wa atsogoleri ena a ndale amene amagwiritsa ntchito misonkhano komanso masamba a mchezo ndi kumafalitsa nkhani zabodza komanso zonyoza atsogoleri anzawo.

Pakadali pano, mfumu yayikulu Kuntaja yayamikira a Kunkuyu kaamba kokhazikitsa chikhochi chomwe adzipikisana matimu a m’mboma la Blantyre.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mponda to strengthen Bullets squad

Romeo Umali

ROYAL FAMILY GATHERS AT BALMORAL AMID CONCERNS FOR QUEEN’S HEALTH

MBC Online

Timu ya Ekhaya ikusendera chifupi ndi ligi

Foster Maulidi
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.