Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi kwa Jenda amanga Boma

Apolisi kwa Jenda m’boma la Mzimba amanga a Robert Boma a zaka 34 atawapeza ndi chamba cholemera ma kilo 32 pamene amafuna kuti akwere nacho basi yopita ku Lilongwe.

Ofalitsankhani ku polisi ya Jenda, a MacFarlen Mseteka, akuti akwanitsa kugwira mkuluyu pambuyo potsinidwa khutu kuti a Boma anali ku Luwawa.

Apolisi atathamangirako, a Boma anathawira mu basi yomwe inali pa depoti.

Atawapeza, anawafufuza ndipo anawapeza ndi Chambacho chomwe sanatulutse msonkho wake, ndipo apolisi sanachedwetse koma kuwamanga kuti akayankhe mlandu.

A Boma ndi a m’mudzi wa Chiphazi kwa mfumu yayikulu Kasumbu m’boma la Dedza.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

K15 Million ndiyomwe ikufunika kuthandizira Peter Mlangeni

Paul Mlowoka

Bullets reach FDH Bank Cup final after historic floodlight victory

MBC Online

FDYD Calls on Government to Bail out Youths with Disabilities

Alick Sambo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.