Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Boma likuyesetsa kutulutsa ma Passport — Zikhale Ng’oma

Nduna yoona chitetezo cha m’dziko, a Ken Zikhale Ng’oma, yati ziphaso zolowera ndi kutulukira m’dziko muno (ma passport) zikhala zikutuluka posachedwapa.

A Zikhale Ng’oma ati izi zili chomwechi chifukwa ntchito yosindikiza ma passport inayamba ndipo akuyesetsa kuti idzifulumira.

Iwo amatsimikizira anthu amene anapita ku ofesi za Immigration mu mzinda wa Blantyre, pamene iwo anakayendera malowa.

Pa tsiku, Immigration ikutulutsa ma passport okwana 500, omwe a Ng’oma ati ndi osakwanira.

Olemba: Charles Chindongo
#MBCDigital
#Video

Related posts

Ayamikira Chitukuko cha milatho

Rabson Kondowe

Mwambo wa Kulamba ulipo chaka chino

McDonald Chiwayula

Tisagulise chimanga chathu chidakali kumunda —Makwangwala

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.