Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Mkulu wa apolisi m’dziko muno, a Merlyne Yolamu, wachenjeza kuti apolisi athana ndi wina aliyense oyambitsa ziwawa panthawi imene zokonzekera zachisankho zili mkati.

A Yolamu apereka chenjezoli pa msonkhano opereka uthenga olimbana ndi nkhanza zosiyanasiyana, omwe unachitikira m’boma la Mzimba pa Jenda.

“Ndichenjeze pano kuti timanga wina aliyense oyambitsa zisokonezo nthawi ino, lolani wina aliyense apange msonkhano wake mwaufulu posazulirana mbendera kapena kemenyana,” anatero a Yolamu.

Iwo anati a Malawi ndi amodzi ngakhale amasiyana zipani kotero anthu sakuyenera kusankhana.

Olemba: Henry Haukeya

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MALAWI TO RAISE K15 BN FROM CEMENT

MBC Online

MBC gets its turn at Parliament

Trust Ofesi

Race to September: Parties intensify nationwide rallies

Chisomo Break
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.