Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Okweza dala mitengo ya katundu nthawi yawo yatha — Mumba

Nduna ya za malonda a Vitumbiko Mumba yachenjeza kuti boma sililekelera kuti aMalawi avutike ndi kukwera kwa mitengo ya zinthu kaamba ka anthu ena adyera.
A Mumba, omwenso adzayime ndi mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera pa 16 September pano, ayankhula izi m’boma la Mzimba pa misonkhano yoyimayima.
Iwo anati boma lili tchelu kuthana ndi wina aliyense yemwe akukwezera dala mitengo ya katundu pofuna kupweteka aMalawi.
Izi zikutsatira malipoti a kupezeka kwa sugar komanso cement zomwe anati anthu ena osakonda dziko lawo amabisira dala, zomwe boma la Dr Chakwera likuthana nazo.
Olemba: Grant Mhango
Print Friendly, PDF & Email

Related posts

One killed in Kasungu road accident

MBC Online

Malawian teacher advocates for scholarships to transform lives

McDonald Chiwayula

Witness in Allan Witika murder to testify in camera

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.