Katswiri ochita zisudzo, Jamil Chikakuda, yemwe amadziwika bwino ndi dzina loti Che Mandota, wati sakufuna kutenga nawonso gawo mu mphotho zosiyanasiyana zimene aluso amapatsidwa m’dziko muno pa chaka kaamba kaluso lawo.
Che Mandota wati akufuna kupereka mpata kwa aluso ena kaamba kakuti iye anatenga mphoto zonse zimene waluso angakhumbire kutenga m’dziko muno.
Kulengezaku kwadza patangopita masiku owerengeka Zeze Kingston nayenso atalengeza ganizo ngati lomweli.