Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Zavuta ku Tunisia!

Malawi yagonja 2-0 ndi Tunisia pa bwalo la masewero la Stade Olympique Hammadi Agebri munzinda wa Tunis. Awa anali masewero a mpira wamiyendo odzigulira malo mumpikisano wa 2026 World Cup.

Zigoli za Tunisia adamwetsa ndi Seifeddine Jaziri pamphindi 86 ndi Elias Achouri pamphindi 90+2 kudzera pa penote. Osewera wa Malawi, Lloyd Aarod, adapatsidwa Red Card mu mphindi 64.

Mwayi wa Flames unapezeka pa mphindi 90+8 kudzera pa penate koma ikakuona litsiro siikata, goloboyi wa Tunisia, Aymen Dahmen, anakwanitsa kuuchotsa penateyo imene anamenya Richard Mbulu.

Zateremu mu gulu H ndiye kuti Flames ili pa nambala 6 ndi ma point 6, pamene Tunisia ikutsogolera gululi ndi ma point 16.

Related posts

UMP Awards decorates MBC presenters

Romeo Umali

Baylor College of Medicine tackles health sector gaps through research

Romeo Umali

MALAWI’S TOUGH FIGHT AGAINST WILDLIFE CRIMES BEARING FRUITS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.