Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tisagwire ntchito monyinyilika -Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati anthu ogwira ntchito m’boma asamagwire ntchito monyinyilika chifukwa zotsatira zogwira ntchito mosadzipereka amavutika ndi aMalawi.

Mtsogoleriyu wati boma lake silisekelera mchitidwe wachipwilikiti komanso kugwira ntchito mosalumikizana ndi maofesi ena.

Dr Chakwera ati sukulu ya MSG ithandiza anthu ogwira ntchito m’boma kuti pogwira ntchito yawo adziika dziko lawo patsogolo.

Mtsogoleriyu walamula kuti Mlembi wamkulu muofesi mwao agwire ntchito ndi alembi a maunduna osiyanasiyana komanso atsogoleri a kampani za boma kuti adzitumiza ogwira ntchito ku sukuluyi kuti aphunzitsidwe bwino zantchito yawo.Tsopano sukuluyi yatsegulidwa kuti itumikire anthu onse m’dziko muno komanso ena ochokera m’maiko a kunja.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MSG drills Mwayiwathu Hospital staff on note-taking, report-writing

MBC Online

EbAM Project to strengthen resilience of vulnerable communities

McDonald Chiwayula

MALAWI SECURES $100 MN FOR STUDENTS’ LOANS

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.