Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tisagwire ntchito monyinyilika -Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati anthu ogwira ntchito m’boma asamagwire ntchito monyinyilika chifukwa zotsatira zogwira ntchito mosadzipereka amavutika ndi aMalawi.

Mtsogoleriyu wati boma lake silisekelera mchitidwe wachipwilikiti komanso kugwira ntchito mosalumikizana ndi maofesi ena.

Dr Chakwera ati sukulu ya MSG ithandiza anthu ogwira ntchito m’boma kuti pogwira ntchito yawo adziika dziko lawo patsogolo.

Mtsogoleriyu walamula kuti Mlembi wamkulu muofesi mwao agwire ntchito ndi alembi a maunduna osiyanasiyana komanso atsogoleri a kampani za boma kuti adzitumiza ogwira ntchito ku sukuluyi kuti aphunzitsidwe bwino zantchito yawo.Tsopano sukuluyi yatsegulidwa kuti itumikire anthu onse m’dziko muno komanso ena ochokera m’maiko a kunja.

Related posts

Titukuka tikakonza misonkho, magetsi — Old Mutual

Romeo Umali

MZUNI intensifies research

Romeo Umali

‘Inmates have rights too’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.