Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Tipitiliza kulumikizitsa anthu omwe anathawa kwawo – MRCS

Bungwe la Malawi Red Cross Society (MRCS) lati lipitiriza ntchito yake yolumikizitsa nzika zomwe zinathawa kwawo zomwe zikukhala pa msasa wa Dzaleka kuti zidzilumikizana komanso kukumana ndi abale awo.

Mlembi wamkulu ku bungweli a Chifundo Kalulu ayakhula izi pa msasa wa Dzaleka pomwe bungweli limaunikila nzika zomwe zinathawa kwawozi momwe zingatsatire ndondomeko zothandizira  kulumikizana ndi abale awo mwaulere.

Iwo ati kuchokera pomwe bungweli linakhazikitsa ndondomekoyi mchaka cha 2012, bungwe la Malawi Red Cross lakwanitsa kulumikizitsa anthu ambiri ndi abale awo.

M’modzi mwa akuluakulu ku nthambi ya boma yoona za anthu omwe anathawa kwawo a Amos Mkandawire ayamikira bungwe la Malawi Red Cross pokhazikitsa ndondomekoyi ponena kuti ithandizira ana amasiye omwe ali pa msasawu kuti athe kulumikizana ndi abale awo ku maiko a kwawo.

 

Olemba: Madalitso Mhango

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

First Lady urges action on education, youth poverty

Mayeso Chikhadzula

MEC plans voter registration ahead of next year’s elections

MBC Online

JENDA POLICE BUST 98 ILLEGAL IMMIGRANTS

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.