Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Tipitiliza kulumikizitsa anthu omwe anathawa kwawo – MRCS

Bungwe la Malawi Red Cross Society (MRCS) lati lipitiriza ntchito yake yolumikizitsa nzika zomwe zinathawa kwawo zomwe zikukhala pa msasa wa Dzaleka kuti zidzilumikizana komanso kukumana ndi abale awo.

Mlembi wamkulu ku bungweli a Chifundo Kalulu ayakhula izi pa msasa wa Dzaleka pomwe bungweli limaunikila nzika zomwe zinathawa kwawozi momwe zingatsatire ndondomeko zothandizira  kulumikizana ndi abale awo mwaulere.

Iwo ati kuchokera pomwe bungweli linakhazikitsa ndondomekoyi mchaka cha 2012, bungwe la Malawi Red Cross lakwanitsa kulumikizitsa anthu ambiri ndi abale awo.

M’modzi mwa akuluakulu ku nthambi ya boma yoona za anthu omwe anathawa kwawo a Amos Mkandawire ayamikira bungwe la Malawi Red Cross pokhazikitsa ndondomekoyi ponena kuti ithandizira ana amasiye omwe ali pa msasawu kuti athe kulumikizana ndi abale awo ku maiko a kwawo.

 

Olemba: Madalitso Mhango

Related posts

Malawi benefits from UK child development programme

Romeo Umali

Where does the Tevet Levy go?

MBC Online

PMRA yatsutsa kuti m’dziko muno muli mankhwala ambiri osavomerezeka

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.