Apasidwa makofi kamba kodyesa anthu nyama ya fisi
Mnyamata wina kwa Nkalo mboma la Chiradzulu amutuwisa ndi zibakera chifukwa chowadyesa anthu am’deralo nyama ya fisi powanamiza kuti ndi ya Ng’ombe.
Dalaivala akunthidwa atagwidwa akuchita zadama
Dalaivala wina ku Blantyre amukuntha kodetsa nkhawa mdela la Kwacha atamupezelela akuchita zachisembwere ndi mai wina mgalimoto lake.
Asekedwa kamba ka nkhuli
Mwamuna wina akumuseka kwa Sub-T.A. Ngwelero m’boma la Zomba kamba ka nkhuli yomwe ali nao.
M'busa agwidwa akusamba usiku panja
Mbusa wampingo wina kwa Mgona A ku Kanengo mu mzinda wa Lilongwe akuyenda mogwetsa nkhope yake pansi chifukwa cha manyazi atamutulukila kuti amasamba usiku uli onse 10 –kokolo kwinaku akuzungulila nyumba.