Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Religion

M’busa apempha anthu kuti athandize osowa

Atsogoleri amipingo ati nkofunika kuti anthu adzipereka thandizo kwa iwo ovutika potsatira mavuto omwe ambiri m’dziko muno akukumana nawo.

M’busa Bishop William Mandhlopa a mpingo wa Family of God International anayankhula izi ku Area 44 mumzinda wa Lilongwe pamwambo opereka nyumba kwa bambo ndi mai George Phiri, amene ndi abusa opuma a mpingo wa Holy Ghost ndipo ndi okalamba.

Iwo anati chimene achitachi chikhale chilimbikitso kwa anthu kuti adzipereka thandizo kwa iwo ovutika.

M’mau awo, bambo ndi mai Phiri anayamika kwambiri m’busayo kaamba ka nyumbayi, ponena kuti moyo okhala pa rent unali ovuta.

Nyumbayo yamangidwa ndi ndalama zokwana K8 million.

#MBCOnlineServices

Related posts

Nsanje youth urged to refrain from political violence

Rabson Kondowe

Apolisi abalalitsa anthu omwe amachita zipolowe pa mpingo wa CCAP wa Mibawa ku Mbayani

Romeo Umali

ACB urges journalists to lead Malawi’s anti-corruption fight

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.