Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Mafumu ku Mzimba apepesa Dr Chakwera

Inkosi ya Makosi Mbelwa V yatsogolera mafumu m’boma la Mzimba kukapepesa President Dr Lazarus Chakwera pa imfa ya amene anali wachiwiri wawo Dr Saulos Chilima pa ngozi ya ndege ndi anthu ena asanu ndi atatu.

Inkosiyi yati mafumuwa ndi okhudzika popeza ngoziyi idachitikira m’dera lawo, mu nkharango ya Chikangawa m’bomalo, ndipo anati ndi kofunika kuwalimbikitsa Dr Chakwera pa nthawiyi kuti apitilire kutsogolera dziko lino ndi kugwira ntchito yawo moyenera.

Adathokonzanso mtsogoleri wa dziko linoyu poonetsetsa kuti akadaulo akafukufuku apeze mayankho pa chomwe chidachititsa ngoziyi.

Inkosi ya Makosi M’belwa V yapemphanso a Malawi kuti alore ngoziyi kulunzanitsa dziko lino ndipo ati avomeleze zotsatira zomwe zingatuluke pa kafukufukuyu kuti zikhale chitonthozo kwa onse.

 

Related posts

Malawi to attend African Consultation Meeting for 3rd United Nations Oceans Summit

McDonald Chiwayula

Malawi wins several awards at COSAFA

Romeo Umali

Malawi set to host 7th Africa-Wide Agricultural Extension Week

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.