Mkulu wina mdera la mfumu Chimaliro mboma la Thyolo wati zangovuta koma banja amalifuna pomwe wasamuka pachikamwini chifukwa cha khalidwe la anthu apa banjapo makamaka ana. Nkhaniyi ikuti mkuluyo anafika pamudzipo zaka zingapo zapitazo ndipo malingana ndi watitumizira nkhaniyi mkuluyo ngodzilimbikira pa ntchito zakumunda. Pachifukwa-chi ataona kuti mpofuna kupitiliza kukhala odzidalira anagula njinga yake yamoto kuti adzichititsa hayala. Koma masiku apitawa anadabwa mwana wake wamwamuna akumuuza momuophyeza kuti amupatse njingayo kuti ikhale yake. Mkuluyo sanavute koma kumulangiza kuti kulibwino apatse ena kuti pamudzipo adzipeza kangachepe. Mwanayo apa analusa mkuyamba kulalatila atate wake powauza kuti iwo ngobwera ndipo akapitiliza ndiza nkutuzo asamuke. Nkhaniyi inakwiitsa kwambiri mkuluyo ndipo usiku anthu ali mtulo anakwakwaza njinga yake nkukailizira kwina uku zinthu zake monga magombeza, majekete komanso ma solar atamangilira. M’mawa kutacha anthu ndi pomwe anazindikira kuti mkamwini wadula waya. Mkazi wa mkuluyo usiku analephera kunyengerela mwamuna wake koma kuti anakanitsitsa ponena kuti ati adzafera za eni. Anthu mderalo adzudzula apabanjapo kuti akhala akulekerela khalidwe la mwanayo zomwe ati zachititsa kuti mkamwini yemwe amathandiza asamuke kuti maiyo atsale padzuwa.
On Thursday, Prince Barbershop took its services to 100 street children from Blantyre City, as one way of motivating them to leave the streets.
Muchanakwaye Mpuluka, the former Chief Executive Officer for Mulhako wa Alhomwe is in Mangochi Police custody for shooting Edward Mbalasa after he caught him with his lover Vanilla Makhuli in bed.
Barely 24 hours after graduating with a Bachelor of Science in Medical Biology with a distinction at the Malawi University of Science and Technology (MUST) on Tuesday, Aisha Senga died in a road accident in Ntcheu on Wednesday.