Malawi Broadcasting Corporation
Development Floods Local Local News Nkhani

Bushiri apereka chimanga kwa mabanja 200 ku Mangochi

Mneneri Shepherd Bushiri wagawa matumba a chimanga kwa mabanja okwana 200 amene anakhudzidwa ndi vuto lakusefukira kwa madzi m’dera la Mfumu yayikulu Nankumba ku Monkey-Bay m’boma la Mangochi.

Ngoziyi itadza, anthu ambiri anathawira ku malo ongoyembekezera otchedwa Nankhwali ndi Sungo.

A Aubrey Kusakala, amene amayankhulira a Bushiri, anati mneneriyu anali okhudzidwa koposa kotero, anaganiza zothandiza anthuwa.

A Kusakala kupereka chimanga kwa okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi

Sub-Traditional Authority Chiwalo, nawo anathokoza a Bushiri kaamba ka zimenezi ndiponso anamema anthu ena akufuna kwabwino kuti achite zomwezi.

Aka ndi kachitatu kuti a Bushiri agawe chimanga m’bomali ndipo padakali pano, ntchito yogawa chimanga chaulere kwa anthu osowa yafikira anthu opyolera 700000 m’ma boma okwana khumi.

Olemba : Miriam Kaliza
#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MARANATHA STAYS PUT

McDonald Chiwayula

Media, aid agencies hoping to enhance partnerships

Simeon Boyce

Elderly women hail Social Cash Transfer programme

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.