Malawi Broadcasting Corporation
Development Floods Local Local News Nkhani

Bushiri apereka chimanga kwa mabanja 200 ku Mangochi

Mneneri Shepherd Bushiri wagawa matumba a chimanga kwa mabanja okwana 200 amene anakhudzidwa ndi vuto lakusefukira kwa madzi m’dera la Mfumu yayikulu Nankumba ku Monkey-Bay m’boma la Mangochi.

Ngoziyi itadza, anthu ambiri anathawira ku malo ongoyembekezera otchedwa Nankhwali ndi Sungo.

A Aubrey Kusakala, amene amayankhulira a Bushiri, anati mneneriyu anali okhudzidwa koposa kotero, anaganiza zothandiza anthuwa.

A Kusakala kupereka chimanga kwa okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi

Sub-Traditional Authority Chiwalo, nawo anathokoza a Bushiri kaamba ka zimenezi ndiponso anamema anthu ena akufuna kwabwino kuti achite zomwezi.

Aka ndi kachitatu kuti a Bushiri agawe chimanga m’bomali ndipo padakali pano, ntchito yogawa chimanga chaulere kwa anthu osowa yafikira anthu opyolera 700000 m’ma boma okwana khumi.

Olemba : Miriam Kaliza
#MBCDigital
#Manthu

Related posts

‘Sustainable land management key in addressing disasters’

MBC Online

Apolisi anjata m’busa pomuganizira kuti anaba zipangizo za ESCOM

Romeo Umali

African Consultation for 3rd UN Ocean Conference underway in Tangier

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.