Malawi Broadcasting Corporation
Development Floods Local Local News Nkhani

Bushiri apereka chimanga kwa mabanja 200 ku Mangochi

Mneneri Shepherd Bushiri wagawa matumba a chimanga kwa mabanja okwana 200 amene anakhudzidwa ndi vuto lakusefukira kwa madzi m’dera la Mfumu yayikulu Nankumba ku Monkey-Bay m’boma la Mangochi.

Ngoziyi itadza, anthu ambiri anathawira ku malo ongoyembekezera otchedwa Nankhwali ndi Sungo.

A Aubrey Kusakala, amene amayankhulira a Bushiri, anati mneneriyu anali okhudzidwa koposa kotero, anaganiza zothandiza anthuwa.

A Kusakala kupereka chimanga kwa okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi

Sub-Traditional Authority Chiwalo, nawo anathokoza a Bushiri kaamba ka zimenezi ndiponso anamema anthu ena akufuna kwabwino kuti achite zomwezi.

Aka ndi kachitatu kuti a Bushiri agawe chimanga m’bomali ndipo padakali pano, ntchito yogawa chimanga chaulere kwa anthu osowa yafikira anthu opyolera 700000 m’ma boma okwana khumi.

Olemba : Miriam Kaliza
#MBCDigital
#Manthu

Related posts

ESCOM, MEAP project to connect over 90,000 customers by June

Rabson Kondowe

SA Govt to determine how many Malawians died in Limpopo accident

Yamikani Simtowe

Region 5 enhances global partnerships

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.