Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Akhazikitsa chipani chatsopano

Malipoti akusonyeza kuti mtsogoleri wambali ya aphungu otsutsa boma kunyumba yamalamulo, a Kondwani Nankhumwa, akhazikitsa chipani chatsopano chotchedwa People’s Development Party (PDP).

Malinga ndi kalata yomwe ayibweretsa poyera kudzera patsamba lawo la mchezo, chipanichi chichititsa msonkhano wa atolankhani posachedwapa kumenenso chidzasonyeze kumtundu wa  aMalawi atsogoleri ake ongogwirizira ma udindo.

A Nankhumwa, omwe ndi phungu wadera la pakati m’boma la Mulanje, adachotsedwa m’chipani cha Democratic Progressive (DPP) miyezi yapitayo.

Related posts

FISCAL POLICE NAB MULLI, MUHARA

MBC Online

Why Malawian players’ foreign moves often end early

Romeo Umali

TISADULE MITENGO MWACHISAWAWA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.