Malawi Broadcasting Corporation
Development Entertainment Local Music News

Zikomo Ambuye — Avokado

Oyimba nyimbo za chamba cha Amapiano, Christopher ‘Avokado’ Malera wayamika Mulungu pomupulumutsa pa ngozi ya galimoto yomwe idachitika Lachiwiri m’mawa ku Mvera m’boma la Dowa.

Asadachite ngozi

Galimoto lake linawombana ndi wa njinga yamoto yemwe akuti amayenda mbali yake.

Atachita ngozi

Koma Avokado wati sanavulale paliponse kupatulapo wanjingayo, amene wavulala mwendo ndipo akulandira thandizo pa chipatala chachikulu cha m’bomalo.

Galimotolo lidatembenuzika katatu

“Ubwino wake ndinamanga lamba wa galimoto langa lomwe linatembenuzika katatu,” iye anatero.

Katswiri oyimbayu posachedwapa adatulutsa nyimbo yotchedwa ‘Msandipitilire Yesu’.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

M’nyamata wa zaka 17 adziombera chifukwa cha chikondi

Charles Pensulo

Parliamentarians call for action on agriculture development at Accra meeting

McDonald Chiwayula

Zokonzekera za Ku Mingoli zili mkati

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.