Malawi Broadcasting Corporation
Development Entertainment Local Music News

Zikomo Ambuye — Avokado

Oyimba nyimbo za chamba cha Amapiano, Christopher ‘Avokado’ Malera wayamika Mulungu pomupulumutsa pa ngozi ya galimoto yomwe idachitika Lachiwiri m’mawa ku Mvera m’boma la Dowa.

Asadachite ngozi

Galimoto lake linawombana ndi wa njinga yamoto yemwe akuti amayenda mbali yake.

Atachita ngozi

Koma Avokado wati sanavulale paliponse kupatulapo wanjingayo, amene wavulala mwendo ndipo akulandira thandizo pa chipatala chachikulu cha m’bomalo.

Galimotolo lidatembenuzika katatu

“Ubwino wake ndinamanga lamba wa galimoto langa lomwe linatembenuzika katatu,” iye anatero.

Katswiri oyimbayu posachedwapa adatulutsa nyimbo yotchedwa ‘Msandipitilire Yesu’.

 

Related posts

Education Ministry for smooth MANEB exams

Romeo Umali

MADAM CHAKWERA VISITS PHALOMBE CYCLONE SURVIVORS

MBC Online

NGO consortium makes progress in ‘Kids Health Kids Rights’ project

Doreen Sonani
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.