Malawi Broadcasting Corporation
Development Entertainment Local Music News

Zikomo Ambuye — Avokado

Oyimba nyimbo za chamba cha Amapiano, Christopher ‘Avokado’ Malera wayamika Mulungu pomupulumutsa pa ngozi ya galimoto yomwe idachitika Lachiwiri m’mawa ku Mvera m’boma la Dowa.

Asadachite ngozi

Galimoto lake linawombana ndi wa njinga yamoto yemwe akuti amayenda mbali yake.

Atachita ngozi

Koma Avokado wati sanavulale paliponse kupatulapo wanjingayo, amene wavulala mwendo ndipo akulandira thandizo pa chipatala chachikulu cha m’bomalo.

Galimotolo lidatembenuzika katatu

“Ubwino wake ndinamanga lamba wa galimoto langa lomwe linatembenuzika katatu,” iye anatero.

Katswiri oyimbayu posachedwapa adatulutsa nyimbo yotchedwa ‘Msandipitilire Yesu’.

 

Related posts

NICE, CCJP lauds Political Empowerment of Women 2024 – 2030 Strategy

Rabson Kondowe

Committee announces closure Tobacco selling season

Romeo Umali

Aloza chala maboma akale posalabadira nsewu wa Karonga-Chiweta

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.