Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Wapolisi wafa pomwe amalimbana ndi mbava

Apolisi m’dziko muno atsimikiza za imfa ya wapolisi mzawo Petros Mhango yemwe amagwira ntchito pa polisi ya Soche ku Blantyre.

Ofalitsankhani zapolisi m’dziko muno, a Peter Kalaya, wati a Mhango afa wapolisi mzawo atawaombera mwangozi pomwe amalimbana ndi mbava ku Chileka mu mzinda womwewo wa Blantyre.

A Kalaya ati apolisi anamvetsedwa kuti anthu ena akonza zokaba kunyumba kwa munthu wina ku Chileka ndipo anathamangira ku maloko komwe anayamba kuwomberana ndi mbavazo.

Mwatsoka, wapolisi wina anaombera a Mhango omwe anatsimikizika kuti afa atafika pachipatala chachikulu cha Queen Elizabeth Central Hospital.

Pakuwomberanako, apolisi awombera ndikupha mbava ziwiri pomwe zina zinathawa.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malemu Kayanula anali Mlangizi

Austin Fukula

National Arts and Heritage Promotion Fund development makes strides

MBC Online

Jiya wayamikira chitukuko, wadzudzula mchitidwe oononga

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.