Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Wapereka mbatata yophika kuti asamuulure kuti wagwilira ana awiri

A Polisi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre anjata a Paul Jalasi azaka 46, powaganizira kuti anagwilirira ana awiri a zaka zisanu ndi zitatu komanso wina wazaka zisanu zokha.

Ofalitsankhani ku Polisiyi, a Aubrey Singanyama, ati a Jalasi anawapatsa anawa mbatata kuti asakaulule pamene adachita mlanduwu ku Bangwe.

A Singanyama ati izi zidachitika pamene amayi a anawa anali kochita malonda ku msika wa Limbe ndipo m’modzi mwa amayiwa anauzidwa za upanduwu ndipo anakamang’ala nkhaniyi ku Polisi kuti bambo amene akumuganizirayu amukwidzinge.

A Jalasi amachoka m’mudzi wa Chingoni kwa mfumu yayikulu Mponda m’boma la Ntcheu.

 

Related posts

MCP ASSURES  DOWA  OF IMPROVED  LIVELIHOODS

Mayeso Chikhadzula

Mudzi Connect uplifts lives in Dowa

Rabson Kondowe

Malawi making stride in girls’ empowerment – First Lady

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.