Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Wapereka mbatata yophika kuti asamuulure kuti wagwilira ana awiri

A Polisi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre anjata a Paul Jalasi azaka 46, powaganizira kuti anagwilirira ana awiri a zaka zisanu ndi zitatu komanso wina wazaka zisanu zokha.

Ofalitsankhani ku Polisiyi, a Aubrey Singanyama, ati a Jalasi anawapatsa anawa mbatata kuti asakaulule pamene adachita mlanduwu ku Bangwe.

A Singanyama ati izi zidachitika pamene amayi a anawa anali kochita malonda ku msika wa Limbe ndipo m’modzi mwa amayiwa anauzidwa za upanduwu ndipo anakamang’ala nkhaniyi ku Polisi kuti bambo amene akumuganizirayu amukwidzinge.

A Jalasi amachoka m’mudzi wa Chingoni kwa mfumu yayikulu Mponda m’boma la Ntcheu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Experts criticise Malawi Queens’ performance at 2025 Africa Netball Cup

MBC Online

US to support Malawi in addressing food shortage

MBC Online

Ensure child safety, care amidst disasters — Gender Minister

Madalitso Mhango
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.