Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Wapereka mbatata yophika kuti asamuulure kuti wagwilira ana awiri

A Polisi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre anjata a Paul Jalasi azaka 46, powaganizira kuti anagwilirira ana awiri a zaka zisanu ndi zitatu komanso wina wazaka zisanu zokha.

Ofalitsankhani ku Polisiyi, a Aubrey Singanyama, ati a Jalasi anawapatsa anawa mbatata kuti asakaulule pamene adachita mlanduwu ku Bangwe.

A Singanyama ati izi zidachitika pamene amayi a anawa anali kochita malonda ku msika wa Limbe ndipo m’modzi mwa amayiwa anauzidwa za upanduwu ndipo anakamang’ala nkhaniyi ku Polisi kuti bambo amene akumuganizirayu amukwidzinge.

A Jalasi amachoka m’mudzi wa Chingoni kwa mfumu yayikulu Mponda m’boma la Ntcheu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Thyolo ramps up efforts to bolster Covid-19 Vaccine uptake

MBC Online

Kaliati’s loss is public mistrust — Political Analysts

MBC Online

NBM donates K2 million to support Business Journalists’ AGM

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.