Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Local Music News Nkhani

Waluso asamatuwe ndi umphawi — Wendy

Mkulu wa Jacobs event, Wendy Harawa, wati chilichonse chili m’chimake pa chikonzero chofuna kubweretsa akatswiri akunja pankhani zamsangulutso kuti adzathandize aluso am’dziko muno za momwe angamachitire kuti adzitha kupindula ndi luso lawo.

Harawa wati ndizomvetsa chisoni kuti aluso ambiri m’dziko muno amakalamba asanadyelere luso lawo poti sadziwa njira zoti akhoza kutsatira kuti apambane ndi luso lawo.

Iye wati ichi ndichifukwa wakonza maphunzirowa.

Ena mwa akatswiri omwe adzakhale nawo ndi Mike Dada, yemwe ndi mtsogoleri wa Afrima Awards ndipo ndikadaulo wa zamalamulo, Ayo Animashaun yemwe ndi mkulu wa Headies Awards, smooth Promotions ndi Hip Tv Komanso Eric Belamy wa Live Nation: Paris, yemwe amathandizira kwambiri akatswiri akunja monga Beyonce, Jay Z, Drake akabwera ku Africa ndi enanso ambiri.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Pact Malawi calls for collaboration in GBV, child abuse cases

Sothini Ndazi

Sendeza commissions 15 CBCCs in Thyolo

Kumbukani Phiri

Goal within reach — Tabitha

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.