Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Walipira chindapusa chifukwa chonyoza wodwala AIDS

Khoti lina ku Balaka lalamula bambo wazaka 45, Frank Nazombe, kuti apereke chindapusa cha ndalama zokwana K65,000 chifukwa chonyoza mayi wodwala matenda a AIDS.

Mneneri wapolisi ku Balaka, a Gladson M’bumpha, wati Nazombe anayambana ndi mayiyo ku mowa.

Tsiku lotsatira, Nazombe analawira mammawa kupita kunyumba kwa mayiyo ndikuyamba kumunena kuti akudwala matenda a AIDS ndipo wafalitsa matendawo kwa amuna ochuluka mderalo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Farmers hail newly opened Phwezi-Uzumara road

MBC Online

MEC urges professionalism in 2025 elections

MBC Online

Living Waters Church feeds senior citizens

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.