Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local Local News Nkhani

Ufa othandizira ovutika ndi njala wafika

Gawo loyamba la ufa umene boma lagula wa ndalama zokwana $20 million othandiza anthu amene akhudzidwa ndi njala tsopano wayamba kufika m’dziko muno.

Boma lagula ufawu kudzera ku bungwe la WFP kuchokera m’maiko a South Africa ndi Tanzania.

Mwambo opereka ufawu ku boma wachitika ku Limbe mu mzinda wa Blantyre.

Mlembi wamkulu mu unduna wa zamalimidwe owona za ulimi wanthilira, a Geoffrey Mamba, ndiwo alandira ufawu ku Limbe kuchokera kwa mkulu wa WFP m’dziko muno, a Paul Turnbull.

Anthu okwana 4.4 million ndiwo akuvutika ndi njala ndipo ufawu onse ukwana ma tani 23,000 ndipo ufikira anthu otere kuyambira mawa loweruka, malinga ndi a Mamba.

 

Related posts

PRISAM commends government for teacher recruitment

McDonald Chiwayula

Nzika ziwiri zadziko la China azimanga zitakomola munthu

Romeo Umali

Sports analyst urges Malawi Beach Soccer to utilise home ground

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.